Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Danieli 5:25 - Buku Lopatulika

Ndipo lemba lolembedwa ndi ili: MENE MENE TEKEL ndi PARSIN.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo lemba lolembedwa ndi ili: MENE MENE TEKEL UFARSIN.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.

Onani mutuwo



Danieli 5:25
10 Mawu Ofanana  

Ndipo anamdzera kalata yofuma kwa Eliya mneneri, ndi kuti, Atero Yehova Mulungu wa Davide atate wanu, Popeza simunayende m'njira za Yehosafati atate wanu, kapena m'njira za Asa mfumu ya Yuda,


Chifumu chako chatsitsidwa kunsi kumanda, ndi phokoso la mingoli yako; mphutsi zayalidwa pansi pa iwe, ndi mphukutu zakukuta.


Chifukwa chake choipa chidzafika pa iwe; sudzadziwa kucha kwake, ndipo chionongeko chidzakugwera; sudzatha kuchikankhira kumbali; ndipo chipasuko chosachidziwa iwe chidzakugwera mwadzidzidzi.


Ndipo amitundu onse adzamtumikira iye, ndi mwana wake, ndi mdzukulu wake, mpaka yafika nthawi ya dziko lake; ndipo amitundu ambiri ndi mafumu aakulu adzamuyesa iye mtumiki wao.


Pamenepo nsonga ya dzanja inatumidwa kuchokera pamaso pake, nililembedwa lembali.


Kumasulira kwake kwa mau awa ndi uku: MENE, Mulungu anawerenga ufumu wanu, nautha.


Sadzauka kodi modzidzimuka iwo amene adzakuluma, ndi kugalamuka iwo amene adzakugwedezetsa; ndipo udzakhala zofunkha zao?


Iye anachita zamphamvu ndi mkono wake; Iye anabalalitsa odzitama ndi mlingaliro wa mtima wao.


Koma Mulungu anati kwa iye, Wopusa iwe, usiku womwe uno udzafunidwa moyo wako; ndipo zinthu zimene unazikonza zidzakhala za yani?


Ndiponso Yehova adzapereka Israele pamodzi ndi iwe m'dzanja la Afilisti; ndipo mawa iwe ndi ana ako mudzakhala kuli ine; Yehova adzaperekanso khamu la Aisraele m'dzanja la Afilisti.