Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 12:20 - Buku Lopatulika

20 Koma Mulungu anati kwa iye, Wopusa iwe, usiku womwe uno udzafunidwa moyo wako; ndipo zinthu zimene unazikonza zidzakhala za yani?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Koma Mulungu anati kwa iye, Wopusa iwe, usiku womwe uno udzafunidwa moyo wako; ndipo zinthu zimene unazikonza zidzakhala za yani?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Koma Mulungu adamuuza kuti, ‘Wopusawe! Usiku womwe uno akulanda moyo wako. Nanga zonse zimene wadzisungirazi zidzakhala za yani?’ ”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 “Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’

Onani mutuwo Koperani




Luka 12:20
35 Mawu Ofanana  

Nawawerengera Hamani kulemera kwake kwakukulu, ndi ana ake ochuluka, ndi zonse mfumu idamkuza nazo, ndi umo adamkweza koposa akalonga ndi anyamata a mfumu.


Pakuti chiyembekezo cha wonyoza Mulungu nchiyani pomlikhatu Mulungu, pomchotsera moyo wake?


Indedi munthu ayenda ngati mthunzi; Indedi avutika chabe: Asonkhanitsa chuma, ndipo sadziwa adzachilandira ndani?


Pakuti aona anzeru amafa, monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo, nasiyira ena chuma chao.


Ha? M'kamphindi ayesedwa bwinja; athedwa konse ndi zoopsa.


Asanathe nacho chokhumba chao, chakudya chao chili m'kamwa mwao,


Chuma cha uchimo sichithangata; koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.


Chuma sichithandiza tsiku la mkwiyo; koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.


Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu; alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi chuma chambiri.


Usanyadire zamawa, popeza sudziwa tsiku lina lidzabala chiyani?


Wochulukitsa chuma chake, pokongoletsa ndi phindu, angokundikira yemwe achitira osauka chisoni.


Idzani inu, ati iwo, ndidzatengera vinyo, ndipo tidzakhuta chakumwa chaukali; ndipo mawa kudzakhala monga tsiku lalero, tsiku lalikulu loposa ndithu.


Monga nkhwali iumatira pa mazira amene sinaikire, momwemo iye amene asonkhanitsa chuma, koma mosalungama; pakati pa masiku ake chidzamsiya iye, ndipo pa chitsirizo adzakhala wopusa.


inu okondwera nacho chopanda pake, ndi kuti, Kodi sitinadzilimbitse tokha ndi kulanda Karinaimu mwa mphamvu yathuyathu?


Pakuti chinkana akunga minga yoyangayanga, naledzera nacho choledzeretsa chao, adzathedwa konse ngati chiputu chouma.


Opusa inu, kodi Iye wopanga kunja kwake sanapangenso m'kati mwake?


Pamene angonena, Mtendere ndi mosatekeseka, pamenepo chionongeko chobukapo chidzawagwera, monga zowawa mkazi wa pakati; ndipo sadzapulumuka konse.


Lamulira iwo achuma m'nthawi ino ya pansi pano, kuti asadzikuze, kapena asayembekezere chuma chosadziwika kukhala kwake, koma Mulungu, amene atipatsa ife zonse kochulukira, kuti tikondwere nazo;


pakuti sitinatenge kanthu polowa m'dziko lapansi, ndiponso sitingathe kupita nako kanthu pochoka pano;


inu amene simudziwa chimene chidzagwa mawa. Moyo wanu uli wotani? Pakuti muli utsi, wakuonekera kanthawi, ndi pamenepo ukanganuka.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa