Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Danieli 10:7 - Buku Lopatulika

Ndipo ine Daniele ndekha ndinaona masomphenyawo; pakuti anthu anali nane sanaone masomphenyawo; koma kunawagwera kunjenjemera kwakukulu, nathawa kubisala.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ine Daniele ndekha ndinaona masomphenyawo; pakuti anthu anali nane sanaone masomphenyawo; koma kunawagwera kunjenjemera kwakukulu, nathawa kubisala.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ine Danieli ndinali ndekha pamene ndinaona masomphenyawa; anthu amene anali ndi ine sanawaone, koma anadzazidwa ndi mantha kotero kuti anathawa ndi kukabisala.

Onani mutuwo



Danieli 10:7
8 Mawu Ofanana  

Ndipo anati, Ndinamva mau anu m'mundamu, ndipo ndinaopa chifukwa ndinali wamaliseche ine; ndipo ndinabisala.


Lowa m'phanga, bisala m'fumbi, kuchokera pa kuopsa kwa Yehova, ndi pa ulemerero wachifumu wake.


Kodi munthu angathe kubisala mobisika kuti ndisamuone iye? Ati Yehova. Kodi Ine sindidzala kumwamba ndi dziko lapansi? Ati Yehova.


Wobadwa ndi munthu iwe, udye mkate wako ndi kunthunthumira, ndi kumwa madzi ako ndi kunjenjemera, ndi kutenga nkhawa;


Ndipo iwo akukhala nane anaonadi kuunika, koma sanamve mau akulankhula nane.


Ndipo amunawo akumperekeza iye anaima duu, atamvadi mau, koma osaona munthu.


ndipo maonekedwewo anali oopsa otere, kuti Mose anati, Ndiopatu ndi kunthunthumira.