Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 6:1 - Buku Lopatulika

Pambuyo pake Davide anamemezanso osankhika onse a mu Israele, anthu zikwi makumi atatu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pambuyo pake Davide anamemezanso osankhika onse a m'Israele, anthu zikwi makumi atatu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Davide adasonkhanitsanso ankhondo okwanira 30,000, amene adaŵasankha pakati pa Aisraele.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Davide anasonkhanitsanso pamodzi ankhondo 3,000 osankhidwa pakati pa Aisraeli.

Onani mutuwo



2 Samueli 6:1
7 Mawu Ofanana  

koma chokhachi anadya anyamata, ndi gawo lao la anthu amene ananka pamodzi ndi ine, Anere, Esikolo, ndi Mamure, iwo atenge gawo lao.


Pomwepo mafuko onse a Israele anabwera kwa Davide ku Hebroni, nalankhula nati, Taonani, ife ndife fupa lanu ndi mnofu wanu.


Pamenepo Solomoni anasonkhanitsa akulu a Israele, ndi akulu onse a mafuko, akalonga a nyumba za atate a ana a Israele, kwa mfumu Solomoni mu Yerusalemu, kukatenga likasa la chipangano cha Yehova m'mzinda wa Davide, ndiwo Ziyoni.


M'mwemo Davide anamemeza Aisraele onse kuyambira Sihori wa ku Ejipito mpaka polowera ku Hamati, kutenga likasa la Mulungu ku Kiriyati-Yearimu.