Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 4:1 - Buku Lopatulika

Ndipo pamene Isiboseti mwana wa Saulo, anamva kuti Abinere adakafera ku Hebroni, manja ake anafooka, ndi Aisraele onse anavutika.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pamene Isiboseti mwana wa Saulo, anamva kuti Abinere adakafera ku Hebroni, manja ake anafooka, ndi Aisraele onse anavutika.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Isiboseti, mwana wa Saulo, atamva kuti Abinere adakafera ku Hebroni, adataya mtima, ndipo Aisraele onse adachita mantha kwambiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.

Onani mutuwo



2 Samueli 4:1
11 Mawu Ofanana  

ndipo ndidzamgwera ali wolema ndi wofooka, ndi kumuopsa; ndi anthu onse amene ali naye adzathawa; pamenepo ndidzakantha mfumu yokha;


Koma Abinere, mwana wa Nere, kazembe wa khamu la ankhondo a Saulo anatenga Isiboseti mwana wa Saulo, namuolotsa nanka naye ku Mahanaimu;


Pofikanso Abinere ku Hebroni, Yowabu anampambutsa kupita naye pakati pa chipata kulankhula naye poduka mphepo; namgwaza pomwepo m'mimba, nafa, chifukwa cha mwazi wa Asahele mbale wake.


Pamenepo anthu a m'dziko anafoketsa manja a anthu Ayuda, nawavuta pomanga,


Pakuti anafuna onse kutiopsa, ndi kuti, Manja ao adzaleka ntchito, ndipo siidzachitika. Koma Inu, Mulungu, mulimbitse manja anga tsopano.


Chifukwa chake manja onse adzafooka, ndi mitima yonse ya anthu idzasungunuka;


Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede.


Mfumu ya ku Babiloni yamva mbiri yao, ndipo manja ake alefuka; wagwidwa ndi nkhawa, ndi zowawa zonga za mkazi alimkudwala.


Tamva ife mbiri yake; manja athu alefuka, yatigwira nkhawa ndi zowawa ngati za mkazi wobala.


Tsiku lomwelo adzati kwa Yerusalemu, Usaopa Ziyoni, manja anu asakhale olefuka.