Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 2:19 - Buku Lopatulika

Ndipo Asahele anapirikitsa Abinere. Ndipo m'kuthamanga kwake sanapatukire kulamanja, kapena kulamanzere, pakutsata Abinere.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Asahele anapirikitsa Abinere.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Iyeyo adathamangitsa Abinere. Pothamangapo sankayang'ana uku ndi uku, maso anali pa Abinere basi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.

Onani mutuwo



2 Samueli 2:19
9 Mawu Ofanana  

Ndipo analipo ana atatu a Zeruya, ndiwo Yowabu, Abisai ndi Asahele. Ndipo Asahele anali waliwiro ngati mbawala.


Pomwepo Abinere anacheuka nati, Kodi ndi iwe Asahele? Iye nayankha, Ndine.


Ndipo Abinere ananena naye, Patuka iwe kulamanja kapena kulamanzere kwako nudzigwirire wina wa anyamatawo, nutenge zida zake. Koma Asahele anakana kupatuka pakumtsata iye.


Pofikanso Abinere ku Hebroni, Yowabu anampambutsa kupita naye pakati pa chipata kulankhula naye poduka mphepo; namgwaza pomwepo m'mimba, nafa, chifukwa cha mwazi wa Asahele mbale wake.


Motero Yowabu ndi Abisai mbale wake adapha Abinere, popeza iye adapha mbale wao Asahele ku Gibiyoni, kunkhondo.


Nachita iye zoongoka pamaso pa Yehova, nayenda m'njira yonse ya Davide kholo lake, osapatukira ku dzanja lamanja kapena kulamanzere.


Usapatuke kudzanja lamanja kapena kulamanzere; suntha phazi lako kusiya zoipa.


Komatu khala wamphamvu, nulimbike mtima kwambiri, kuti usamalire kuchita monga mwa chilamulo chonse anakulamuliracho Mose mtumiki wanga; usachipatukire ku dzanja lamanja kapena kulamanzere, kuti ukachite mwanzeru kulikonse umukako.


Koma mulimbike mtima kwambiri kusunga ndi kuchita zonse zolembedwa m'buku la chilamulo cha Mose, osachipatukira kulamanja kapena kulamanzere;