Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 15:13 - Buku Lopatulika

Ndipo mthenga unafika kwa Davide nuti, Mitima ya anthu a Israele itsata Abisalomu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo mthenga unafika kwa Davide nuti, Mitima ya anthu a Israele itsata Abisalomu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsiku lina wamthenga adafika kwa Davide kudzanena kuti, “Aisraele onse ali pambuyo pa Abisalomu.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Munthu wina anabweretsa uthenga ndi kudzamuwuza Davide kuti, “Mitima ya Aisraeli onse ili pa Abisalomu.”

Onani mutuwo



2 Samueli 15:13
7 Mawu Ofanana  

Abisalomu anachitira zotero Aisraele onse akudza kwa mfumu kuti aweruze mlandu wao; chomwecho Abisalomu anakopa mitima ya anthu a Israele.


Ndipo anthu onse anachisamalira, ndipo chinawakomera; zilizonse adazichita mfumu zidakomera anthu onse.


Yehova! Ha! Achuluka nanga akundisautsa ine! Akundiukira ine ndi ambiri.


Indetu, anthu achabe ndi mpweya, ndipo anthu aakulu ndi bodza, pakuwayesa apepuka; onse pamodzi apepuka koposa mpweya.


Ndipo mipingo yakumtsogolera ndi yakumtsatira, inafuula, kuti, Hosana kwa Mwana wa Davide! Wolemekezeka ndiye wakudza m'dzina la Ambuye! Hosana mu Kumwambamwamba!


Pilato ananena kwa iwo, Nanga ndidzachita chiyani ndi Yesu, wotchedwa Khristu? Onse anati, Apachikidwe pamtanda.


Pamenepo abale a amake anamnenera mau awa onse m'makutu a eni ake onse a Sekemu; ndi mitima yao inalunjika kutsata Abimeleki; pakuti anati, Ndiye mbale wathu.