Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 1:22 - Buku Lopatulika

Uta wa Yonatani sunabwerere, ndipo lupanga la Saulo silinabwerere chabe, pa mwazi wa ophedwa, pa mafuta a amphamvuwo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Uta wa Yonatani sunabwerera, ndipo lupanga la Saulo silinabwerera chabe, pa mwazi wa ophedwa, pa mafuta a amphamvuwo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Uta wa Yonatani sudabwereko chabe osakhetsa magazi a anthu osabayako ankhondo amphamvu. Ndipo lupanga la Saulo silidabwereko chabe osapha anthu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.

Onani mutuwo



2 Samueli 1:22
7 Mawu Ofanana  

Pakuti, taonani, ndidzabukitsa ndidzafikitsa kudzamenyana ndi Babiloni msonkhano wa mitundu yaikulu kuchokera kudziko la kumpoto; ndipo adzaguba pomenyana ndi iye; kumeneko Babiloni adzachotsedwa; mivi yao idzakhala ngati ya munthu wamaluli wamphamvu; yosabwera chabe.


Mivi yanga ndiiledzeretsa nao mwazi, ndi lupanga langa lidzalusira nyama; ndi mwazi wa ophedwa ndi ogwidwa, ndi mutu wachitsitsi wa mdani.


Ndipo pamene Saulo atakhazikitsa ufumu wa pa Israele, iye anaponyana ndi adani ake onse pozungulira ponse, ndi Mowabu, ndi ana a Amoni, ndi Edomu ndi mafumu a Zoba, ndi Afilisti; ndipo paliponse anapotolokerapo, anawalanga.


Ndipo iye anakula mphamvu, nakantha Aamaleke, napulumutsa Aisraele m'manja a akuwawawanya.


Ndipo Yonatani anavula malaya ake anali nao, napatsa Davide, ndi zovala zake, ngakhale lupanga lake, ndi uta wake, ndi lamba lake.