Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 3:4 - Buku Lopatulika

Pamenepo Yehova anaitana Samuele; ndipo iye anayankha kuti, Ndili pano.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo Yehova anaitana Samuele; ndipo iye anayankha kuti, Ndili pano.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Chauta adaitana kuti, “Samuele, Samuele!” Iye adayankha kuti, “Ŵaŵa!”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”

Onani mutuwo



1 Samueli 3:4
10 Mawu Ofanana  

Ndipo panali zitapita zimenezo, Mulungu anamuyesa Abrahamu nati kwa iye, Abrahamu; ndipo anati, Ndine pano.


Koma mthenga wa Yehova anamuitana iye ndi mau odzera kumwamba, nati, Abrahamu, Abrahamu; ndi iye anati, Ndine pano.


Mwa ansembe ake muli Mose ndi Aroni, ndi Samuele mwa iwo akuitanira dzina lake; anaitana kwa Yehova, ndipo Iye anawayankha.


Pamene Yehova anaona kuti adapatuka kukapenya, Mulungu ali m'kati mwa chitsamba, anamuitana, nati, Mose, Mose. Ndipo anati, Ndili pano.


Ndipo ndinamva mau a Ambuye akuti, Ndidzatumiza yani, ndipo ndani adzatimukira ife? Ndipo ine ndinati, Ndine pano; munditumize ine.


ndipo anagwa pansi, namva mau akunena naye, Saulo, Saulo, Undilondalonderanji?


Ndipotu Mulungu anaika ena mu Mpingo, poyamba atumwi, achiwiri aneneri, achitatu aphunzitsi, pamenepo zozizwa, pomwepo mphatso za machiritso, mathandizo, maweruziro, malilime a mitundumitundu.


Ndipo anathamangira kwa Eli nati, Ndine, popeza mwandiitana ine. Ndipo iye anati, Sindinaitane, kagone. Napita iye, nagona.