Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 6:5 - Buku Lopatulika

5 Ndamvanso kubuula kwa ana a Israele, amene Aejipito awayesa akapolo; ndipo ndakumbukira chipangano changa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Ndamvanso kubuula kwa ana a Israele, amene Aejipito awayesa akapolo; ndipo ndakumbukira chipangano changa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Tsopano ndamva kudandaula kwa Aisraele, amene ali mu ukapolo wa Aejipito, ndipo ndakumbukira chipangano changa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 6:5
11 Mawu Ofanana  

Ndipo Mulungu anakumbukira Nowa ndi zamoyo zonse, ndi nyama zonse zimene zinali pamodzi naye m'chingalawamo; ndipo Mulungu anapititsa mphepo padziko lapansi, naphwa madzi;


ndipo ndidzakumbukira pangano langa limene lili ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo; ndipo madzi sadzakhalanso konse chigumula chakuononga zamoyo zonse.


Akumbukira chipangano chake kosatha, mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;


Ndipo kunali pakupita masiku ambiri aja, idafa mfumu ya Aejipito; ndi ana a Israele anatsitsa moyo chifukwa cha ukapolo wao, nalira, ndi kulira kwao kunakwera kwa Mulungu chifukwa cha ukapolowo.


Ndipo Mulungu anamva kubuula kwao, ndi Mulungu anakumbukira chipangano chake ndi Abrahamu, ndi Isaki, ndi Yakobo.


Ndipo Yehova anati, Ndapenyetsetsa mazunzo a anthu anga ali mu Ejipito, ndamvanso kulira kwao chifukwa cha akuwafulumiza; pakuti ndidziwa zowawitsa zao;


Ndipo mfumu ya Aejipito inanena nao, Inu, Mose ndi Aroni, chifukwa ninji mumasulira anthu ntchito zao? Mukani ku akatundu anu.


M'mazunzo ao onse Iye anazunzidwa, ndipo mthenga wakuimirira pamaso pake anawapulumutsa; m'kukonda kwake ndi m'chisoni chake Iye anawaombola, nawabereka nawanyamula masiku onse akale.


Anathangatira Israele mnyamata wake, kuti akakumbukire chifundo,


Kuchitira atate athu chifundo, ndi kukumbukira pangano lake lopatulika;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa