Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yoweli 2:8 - Buku Lopatulika

Sakankhana, ayenda lililonse m'mopita mwake; akagwa m'zida, siithyoka nkhondo yao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Sakankhana, ayenda lililonse m'mopita mwake; akagwa m'zida, siithyoka nkhondo yao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Sakukankhanakankhana, aliyense akuyenda molunjika. Akupyola pakati pa zida zankhondo, osaŵaimitsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.

Onani mutuwo



Yoweli 2:8
11 Mawu Ofanana  

Ndipo anaika anthu onse, yense ndi chida chake m'dzanja lake, amzinge mfumu, kuyambira mbali ya kudzanja lamanja la nyumba kufikira mbali ya kudzanja lamanzere la nyumba, kuloza kuguwa la nsembe ndi kunyumba.


Ndipo analimbika mtima, namangitsa linga lonse mopasuka, nalikweza mpaka pansanja, ndi linga lina kunja kwake, nalimbitsa Milo m'mzinda wa Davide, napanga zida ndi zikopa zochuluka.


Iwo omanga linga, ndi iwo osenza katundu, posenza, anachita aliyense ndi dzanja lake lina logwira ntchito, ndi lina logwira chida;


Ndipo ine, ndi abale anga, ndi anyamata anga, angakhale amuna olindirira onditsata ine, nnena mmodzi yense wa ife anavula zovala zake, yense anapita ndi chida chake kumadzi.


kuti amletse angaonongeke, ndi moyo wake ungatayike ndi lupanga.


Koma akapanda kumvera adzatayika ndi lupanga, nadzatsirizika osadziwa kanthu.


Dzombe lilibe mfumu, koma lituluka lonse mabwalomabwalo.


Mphukira zako ndi munda wamakangaza, ndi zipatso zofunika, bonongwe ndi narido.


palibe amene adzalema, kapena adzaphunthwa mwa iwo, palibe amene adzaodzera kapena kugona tulo; ngakhale lamba la m'chuuno mwao silidzamasuka, kapena chomangira cha nsapato zao sichidzaduka;


Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda lililonse njira yake, osasokonezeka m'mabande ao.


Alumphira mzinda, athamanga palinga, akwerera nyumba, alowera pamazenera ngati khungu.