Ndipo mfumu inalamulira anthu onse, kuti, Mchitireni Yehova Mulungu wanu Paska, monga mulembedwa m'buku ili la chipangano.
Numeri 9:2 - Buku Lopatulika Ana a Israele achite Paska pa nyengo yoikidwa. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ana a Israele achite Paska pa nyengo yoikidwa. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa “Aisraele azichita Paska pa nthaŵi yake. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero “Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika. |
Ndipo mfumu inalamulira anthu onse, kuti, Mchitireni Yehova Mulungu wanu Paska, monga mulembedwa m'buku ili la chipangano.
Pamenepo Yosiya anachitira Yehova Paska mu Yerusalemu, naphera Paska tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi woyamba.
Tsiku lakhumi ndi chinai la mweziwo, madzulo, muziuchita, pa nyengo yake yoikidwa; muuchite monga mwa malemba ake onse, ndi maweruzo ake onse.
Ndipo tsiku loyamba la mikate yopanda chotupitsa, pamene amapha Paska, ophunzira ananena naye, Mufuna tinke kuti, tikakonze mkadyereko Paska?
Ndipo tsiku la mikate yopanda chotupitsa linafika, limene inayenera kuphedwa nsembe ya Paska.
Ndipo ana a Israele anamanga misasa ku Giligala; nachita Paska tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi, madzulo, m'zidikha za Yeriko.