Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 9:19 - Buku Lopatulika

Ndipo pakukhalitsa mtambo masiku ambiri pamwamba pa chihema, pamenepo ana a Israele anasunga udikiro wa Yehova osayenda ulendo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pakukhalitsa mtambo masiku ambiri pamwamba pa Kachisi, pamenepo ana a Israele anasunga udikiro wa Yehova osayenda ulendo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngakhale mtambowo ukhale masiku ambiri pamwamba pa chihemacho, Aisraele ankasungabe lamulo la Chauta, ndipo sankanyamuka.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.

Onani mutuwo



Numeri 9:19
7 Mawu Ofanana  

koma ukapanda kukwera mtambo, samayenda ulendo wao kufikira tsiku loti wakwera.


Ndipo mukhale pakhomo pa chihema chokomanako masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku, ndi kusunga chilangizo cha Yehova, kuti mungafe; pakuti anandiuza kotero.


Atero Yehova wa makamu: Ukadzayenda m'njira zanga, ndi kusunga udikiro wanga, pamenepo udzaweruza nyumba yanga, ndi kusunga mabwalo anga, ndipo ndidzakupatsa malo oyendamo mwa awa oimirirapo.


Ndipo asunge zipangizo zonse za chihema chokomanako, ndi udikiro wa ana a Israele, kuichita ntchito ya Kachisi.


Pakuwauza Yehova ana a Israele amayenda ulendo, powauza Yehova amamanga mahema ao; masiku onse mtambo ukakhala pamwamba pa chihema amakhala m'chigono.


Ndipo pokhala mtambo pamwamba pa chihema masiku pang'ono; pamenepo anakhala m'chigono monga awauza Yehova, nayendanso ulendo monga anauza Yehova.