Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 33:2 - Buku Lopatulika

Ndipo Mose analembera matulukidwe ao monga mwa maulendo ao, monga mwa mau a Yehova; ndipo maulendo ao ndi awa monga mwa matulukidwe ao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Mose analembera matulukidwe ao monga mwa maulendo ao, monga mwa mau a Yehova; ndipo maulendo ao ndi awa monga mwa matulukidwe ao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mose adalemba maina a malo onse oyambira ulendo ndi chigono chilichonse, monga Chauta adamlamula. Zigono zake potsata malo oyambira ulendo wao zinali motere:

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:

Onani mutuwo



Numeri 33:2
8 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anati kwa Mose, Lembera ichi m'buku, chikhale chikumbutso, nuchimvetse Yoswa; kuti ndidzafafaniza konse chikumbukiro cha Amaleke pansi pa thambo.


Potero anayamba ulendo wao monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose.


Mukalizanso chokweza, a m'zigono za kumwera ayende; alize chokweza pakumuka.


Maulendo a ana a Israele amene anatuluka m'dziko la Ejipito monga mwa makamu ao, ndi dzanja la Mose ndi Aroni, ndi awa.


Ndipo anachokera ku Ramsesi mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi woyamba; atachita Paska m'mawa mwake ana a Israele, anatuluka ndi dzanja lokwezeka pamaso pa Aejipito onse,


Ulendo wake wochokera ku Horebu wofikira ku Kadesi-Baranea, wodzera njira ya phiri la Seiri, ndiwo wa masiku khumi ndi limodzi.


Ndipo Yehova anati kwa ine, Uka, tenga ulendo pamaso pa anthu; kuti alowe ndi kulandira dzikoli ndinalumbirira makolo ao kuti ndidzawapatsa.