Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mlaliki 7:3 - Buku Lopatulika

Chisoni chiposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chisoni chiposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chisoni nchabwino kupambana chimwemwe, chifukwa ngakhale nkhope ikhale yakugwa, mtima umathabe kutolapo nzeru.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.

Onani mutuwo



Mlaliki 7:3
21 Mawu Ofanana  

Ndisanazunzidwe ndinasokera; koma tsopano ndisamalira mau anu.


Kundikomera kuti ndinazunzidwa; kuti ndiphunzire malemba anu.


Ndinati, Kuseka ndi masala; ndi chimwemwe kodi chichita chiyani?


Mtima wa anzeru uli m'nyumba ya maliro; koma mtima wa zitsiru uli m'nyumba ya kuseka.


Nati, Munthu wokondedwatu iwe, Usaope, mtendere ukhale nawe; limbika, etu limbika. Ndipo pamene ananena ndi ine ndinalimbikitsidwa, ndinati, Anene mbuye wanga; pakuti mwandilimbikitsa.


Odala inu akumva njala tsopano; chifukwa mudzakhuta. Odala inu akulira tsopano; chifukwa mudzaseka.


Tsoka inu okhuta tsopano! Chifukwa mudzamva njala. Tsoka inu, akuseka tsopano! Chifukwa mudzachita maliro ndi kulira misozi.


Pakuti chisautso chathu chopepuka cha kanthawi chitichitira ife kulemera koposa kwakukulu ndi kosatha kwa ulemerero;