Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 9:7 - Buku Lopatulika

Koma Yehova akhala chikhalire, anakonzeratu mpando wachifumu wake kuti aweruze.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma Yehova akhala chikhalire, anakonzeratu mpando wachifumu wake kuti aweruze.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Chauta amakhala pa mpando wake waufumu nthaŵi zonse, adakhazika mpando wake kuti aziweruza.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.

Onani mutuwo



Masalimo 9:7
10 Mawu Ofanana  

Koma Inu, Yehova, mukhalabe kunthawi yonse; ndi chikumbukiro chanu ku mibadwomibadwo.


Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba; ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo.


Chilungamo ndi chiweruzo ndiwo maziko a mpando wanu wachifumu; chifundo ndi choonadi zitsogolera pankhope panu.


Asanabadwe mapiri, kapena musanalenge dziko lapansi, ndi lokhalamo anthu, inde, kuyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha, Inu ndinu Mulungu.


Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi kunthawi zonse.


Koma ichi chimodzi musaiwale, okondedwa inu, kuti tsiku limodzi likhala kwa Ambuye ngati zaka chikwi, ndi zaka chikwi ngati tsiku limodzi.


Ndipo ndinaona, mpando wachifumu waukulu woyera, ndi Iye wakukhalapo, amene dziko ndi m'mwamba zinathawa pamaso pake, ndipo sanapezedwe malo ao.