Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 67:6 - Buku Lopatulika

Dziko lapansi lapereka zipatso zake, Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Dziko lapansi lapereka zipatso zake, Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nthaka yabereka zipatso zake, Mulungu, Mulungu wathu watidalitsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.

Onani mutuwo



Masalimo 67:6
13 Mawu Ofanana  

Ndipo ndidzalimbitsa pangano langa ndi Ine ndi iwe pa mbeu zako za pambuyo pako m'mibadwo yao, kuti likhale pangano la nthawi zonse, kuti ndikhale Mulungu wako ndi wa mbeu zako za pambuyo pako.


Pakuti Mulungu ameneyo ndiye Mulungu wathu kunthawi za nthawi, adzatitsogolera kufikira imfa.


Ndipo Mulungu ananenanso kwa Mose, Ukatero ndi ana a Israele, Yehova Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isaki, ndi Mulungu wa Yakobo anandituma kwa inu; ili ndi dzina langa nthawi yosatha, ichi ndi chikumbukiro changa m'mibadwomibadwo.


Ngati inu muli ofuna ndi omvera, mudzadya zabwino za dziko,


Nthawi yomweyo, ati Yehova, ndidzakhala Mulungu wa mabanja onse a Israele, ndipo iwo adzakhala anthu anga.


Koma ili ndi pangano limene ndidzapangana ndi nyumba ya Israele atapita masiku aja, ati Yehova; ndidzaika chilamulo changa m'kati mwao, ndipo m'mtima mwao ndidzachilemba; ndipo ndidzakhala Mulungu wao, nadzakhala iwo anthu anga;


Dziko lidzaperekanso zipatso zake, ndipo mudzadya ndi kukhuta, ndi kukhalamo okhazikika.


ndidzakupatsani mvula m'nyengo zake, ndi dziko lidzapereka zipatso zake, ndi mitengo ya m'minda idzabala zipatso zake.