Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 41:3 - Buku Lopatulika

Yehova adzamgwiriziza pa kama wodwalira; podwala iye mukonza pogona pake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova adzamgwiriziza pa kama wodwalira; podwala iye mukonza pogona pake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta adzamthandiza munthuyo akamadwala. Adzamchiritsa matenda ake onse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.

Onani mutuwo



Masalimo 41:3
7 Mawu Ofanana  

Ndipo ananena nayo, Atero Yehova, Popeza watuma mithenga kukafunsira kwa Baala-Zebubi mulungu wa ku Ekeroni, kodi ndi popeza palibe Mulungu mwa Israele kufunsira mau ake? Chifukwa chake sudzatsika pakama pamene wakwerapo, koma udzafa ndithu.


Ndipo inanena naye, Munthu anakwera kukomana nafe, nati kwa ife, Kabwerereni kwa mfumu imene inakutumani inu, nimunene nayo, Atero Yehova, Kodi ndi popeza palibe Mulungu mwa Israele, kuti ulikutuma kukafunsira kwa Baala-Zebubi mulungu wa ku Ekeroni? Chifukwa chake sudzatsika pakama pamene wakwerapo, koma udzafa ndithu.


Likatha thupi langa ndi mtima wanga, Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga, ndi cholandira changa chosatha.


Ndipo Yehova anatilamulira tizichita malemba awa onse, kuopa Yehova Mulungu wathu, kuti tipindule nako masiku onse, kuti atisunge amoyo, monga lero lino.