Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 32:9 - Buku Lopatulika

Musakhale monga kavalo, kapena ngati bulu, wopanda nzeru; zomangira zao ndizo cham'kamwa ndi chapamutu zakuwakokera, pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Musakhale monga kavalo, kapena ngati bulu, wopanda nzeru; zomangira zao ndizo cham'kamwa ndi chapamutu zakuwakokera, pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Musakhale opanda nzeru ngati kavalo kapena bulu amene ayenera kumuwongolera ndi chitsulo cham'kamwa ndi chapamutu, chifukwa ukapanda kutero, nyamazo sizidzakumvera.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.

Onani mutuwo



Masalimo 32:9
9 Mawu Ofanana  

Pakuti anamasula nsinga zao, nandizunza; anataya chomangira m'kamwa mwao pamaso panga.


wakutilangiza ife koposa nyama za padziko, wakutipatsa nzeru zoposa mbalame za m'mlengalenga?


Ndani adzasenda chovala chake chakunja? Adzalowa ndani kumizere iwiri ya mano ake?


Chikoti chiyenera kavalo, ndi cham'kamwa chiyenera bulu, ndi nthyole iyenera pamsana pa zitsiru.


Kumva ndamva Efuremu alinkulirira kotero, Mwandilanga ine, ndipo ndalangidwa, monga mwanawang'ombe wosazolowera goli; munditembenuze ine, ndipo ine ndidzatembenuka; pakuti inu ndinu Yehova Mulungu wanga.


Pakuti anthu anga apusa, sandidziwa Ine; ali ana opulukira sazindikira; ali ochenjera kuchita choipa koma kuchita chabwino sakudziwa.


Koma ngati tiikira akavalo zogwirira m'kamwa mwao atimvere, tipotolozanso thupi lao lonse.