Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 15:3 - Buku Lopatulika

Ndipo ansembe aakulu anamnenera Iye zinthu zambiri.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ansembe aakulu anamnenera Iye zinthu zambiri.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Akulu a ansembe aja adayamba kumneneza zambiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akulu a ansembe anamunenera zinthu zambiri.

Onani mutuwo



Marko 15:3
11 Mawu Ofanana  

Inde ndikunga munthu wosamva, ndipo m'kamwa mwanga mulibe makani.


Iye anatsenderezedwa koma anadzichepetsa yekha osatsegula pakamwa pake; ngati nkhosa yotsogoleredwa kukaphedwa, ndi ngati mwanawankhosa amene ali duu pamaso pa omsenga, motero sanatsegule pakamwa pake.


Ndipo pakumnenera Iye ansembe aakulu ndi akulu, Iye sanayankhe kanthu.


Ndipo Pilato anamfunsa Iye, Kodi ndiwe mfumu ya Ayuda? Ndipo anayankha, nanena naye, Mwatero.


Ndipo Pilato anamfunsanso, nanena, Suyankha kanthu kodi? Taona, akunenera Iwe zinthu zambiri zotere.


Koma Yesu sanayankhenso kanthu; kotero kuti Pilato anazizwa.


Pa ichi Pilato anafuna kumasula Iye; koma Ayuda anafuula, ndi kunena, Ngati mumasula ameneyo, simuli bwenzi la Kaisara; yense wodziyesera yekha mfumu atsutsana naye Kaisara.