Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 1:54 - Buku Lopatulika

Anathangatira Israele mnyamata wake, kuti akakumbukire chifundo,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Anathangatira Israele mnyamata wake, kuti akakumbukire chifundo,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Wadzathandiza anthu ake Aisraele, pokumbukira chifundo chake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.

Onani mutuwo



Luka 1:54
16 Mawu Ofanana  

Mulungu ali m'kati mwake, sudzasunthika, Mulungu adzauthandiza mbandakucha.


Anakumbukira chifundo chake ndi chikhulupiriko chake kunyumba ya Israele; malekezero onse a dziko lapansi anaona chipulumutso cha Mulungu wathu.


Kumbukira zinthu izi, Yakobo; ndi Israele, pakuti iwe ndiwe mtumiki wanga; ndakuumba, iwe ndiwe mtumiki wanga, Israele, sindidzakuiwala.


Kodi Efuremu ndiye mwana wanga wokondedwa? Kodi ndiye mwana wokondweretsa? Nthawi zonse zoti ndimnenera zomtsutsa, pakuti ndimkumbukiranso ndithu; chifukwa chake mumtima mwanga ndimlirira; ndidzamchitiradi chifundo, ati Yehova.


Yehova anaonekera kwa ine kale, ndi kuti, Inde, ndakukonda iwe ndi chikondi chosatha; chifukwa chake ndakukoka iwe ndi kukukomera mtima.


Mudzapatsa kwa Yakobo choonadi, ndi kwa Abrahamu chifundo chimene munalumbirira makolo athu kuyambira masiku a kale lomwe.


Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino, ndipo eni chuma anawachotsa opanda kanthu.


(Monga analankhula kwa makolo athu) kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yake kunthawi yonse.