Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Hoseya 8:3 - Buku Lopatulika

Israele wachitaya chokoma, mdani adzamlondola.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Israele wachitaya chokoma, mdani adzamlondola.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Aisraele akana zabwino. Nchifukwa chake adani ao adzaŵapirikitsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.

Onani mutuwo



Hoseya 8:3
10 Mawu Ofanana  

Mau a pakamwa pake ndiwo opanda pake ndi onyenga, waleka kuzindikira ndi kuchita bwino.


mudzawalondola mokwiya ndi kuwaononga pansi pa thambo la Yehova.


Otilondola anaposa ziombankhanga za m'mlengalenga m'liwiro lao, anatithamangitsa pamapiri natilalira m'chipululu.


Adzafuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisraele tikudziwani.


Analonga mafumu, koma sikunachokera kwa Ine; anaika akalonga, koma sindinadziwa; anadzipangira mafano a siliva wao ndi golide wao, kuti akalikhidwe.


Kunena za iwo akutsalira, ndidzalonga kukomoka kumtima kwao m'maiko a adani ao; ndi liu la tsamba lotengeka ndi mphepo lidzawapirikitsa; ndipo adzathawa monga amathawa lupanga; ndipo adzagwa wopanda wakuwalondola.


Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Edomu, kapena zinani, sindidzabweza kulanga kwake; popeza analondola mphwake ndi lupanga, nafetsa chifundo chake chonse, ndi mkwiyo wake unang'amba ching'ambire nasunga mkwiyo wake chisungire;


Yehova adzalola adani anu akukantheni; mudzawatulukira njira imodzi, koma mudzawathawa pamaso pao njira zisanu ndi ziwiri, ndipo mudzagwedezeka pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.


pokhala nacho chitsutso, popeza adataya chikhulupiriro chao choyamba.