Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Hoseya 8:2 - Buku Lopatulika

2 Adzafuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisraele tikudziwani.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Adzafuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisraele tikudziwani.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Amalirira kwa Ine kuti ndiŵathandize, amati, ‘Ife Aisraele tikukudziŵani Inu Mulungu wathu.’

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’

Onani mutuwo Koperani




Hoseya 8:2
14 Mawu Ofanana  

Nati iye, Tiye nane, ukaone changu changa cha kwa Yehova. M'mwemo anamuyendetsa m'galeta wake.


Koma Yehu sanazileke zoipa za Yerobowamu mwana wa Nebati, zimene adachimwitsa nazo Israele, ndizo anaang'ombe agolide okhala mu Betele ndi mu Dani.


Musakhulupirire mau onama, kuti, Kachisi wa Yehova, Kachisi wa Yehova, Kachisi wa Yehova ndi awa.


Ndidzamuka ndi kubwerera kunka kumalo kwanga, mpaka adzavomereza kupalamula kwao, nafunafuna nkhope yanga; m'msauko mwao adzandifunafuna mwachangu.


Israele wachitaya chokoma, mdani adzamlondola.


Akulu ake aweruza chifukwa cha mphotho, ndi ansembe ake aphunzitsa chifukwa cha malipo, ndi aneneri ake alosa chifukwa cha ndalama; koma atsamira pa Yehova, nati, Kodi Yehova sali pakati pa ife? Palibe choipa chodzatigwera.


Koma pambuyo pake anadzanso anamwali enawo, nati, Mbuye, mbuye, mutitsegulire ife.


Si yense wakunena kwa Ine, Ambuye, Ambuye, adzalowa mu Ufumu wa Kumwamba; koma wakuchitayo chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba.


Pamene atauka mwini nyumba natseka pakhomo, ndipo inu mudzayamba kuima pabwalo, ndi kugogoda pachitseko, ndi kunena, Ambuye titsegulireni ife; ndipo Iye adzayankha nadzati ndi inu, Sindidziwa inu kumene muchokerako;


Avomereza kuti adziwa Mulungu, koma ndi ntchito zao amkana Iye, popeza ali onyansitsa, ndi osamvera, ndi pa ntchito zonse zabwino osatsimikizidwa.


Iye wakunena kuti, Ndimdziwa Iye, koma wosasunga malamulo ake, ali wabodza, ndipo mwa iye mulibe choonadi;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa