Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 48:13 - Buku Lopatulika

Ndipo Yosefe anatenga iwo onse awiri, Efuremu m'dzanja lake lamanja ku dzanja lamanzere la Yakobo, ndi Manase m'dzanja lake lamanzere ku dzanja lamanja la Israele, nadza nao pafupi ndi iye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Yosefe anatenga iwo onse awiri, Efuremu m'dzanja lake lamanja ku dzanja lamanzere la Yakobo, ndi Manase m'dzanja lake lamanzere ku dzanja lamanja la Israele, nadza nao pafupi ndi iye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yosefe adaŵagwira padzanja anawo, Efuremu ku dzanja lamanja kuti pakutero akhale ku dzanja lamanzere la Yakobe. Manase adakhala kumanzere kuti pakutero akhale ku dzanja lamanja la Yakobe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.

Onani mutuwo



Genesis 48:13
6 Mawu Ofanana  

Ndipo Yosefe anamutcha dzina la woyamba Manase, chifukwa anati iye, Mulungu wandiiwalitsa ine zovuta zanga zonse, ndi nyumba yonse ya atate wanga.


Kwa Yosefe kunabadwa m'dziko la Ejipito Manase ndi Efuremu, amene Asenati mwana wamkazi wa Potifera wansembe wa Oni anambalira iye.


Ndipo Yosefe anatulutsa iwo pakati pa maondo ake, nawerama ndi nkhope yake pansi.


Ndipo Israele anatambalitsa dzanja lake lamanja, naliika pamutu wa Efuremu, amene ndiye wamng'ono, ndi dzanja lake lamanzere pamutu wa Manase, anapingasitsa manja ake dala; chifukwa Manase anali woyamba.


Ana aamuna a Yosefe monga mwa mabanja ao ndiwo: Manase ndi Efuremu.


nadzakhalitsa nkhosa kudzanja lake lamanja, koma mbuzi kulamanzere.