Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 45:4 - Buku Lopatulika

Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, Muyandikiretu kwa ine; nayandikira. Ndipo iye anati, Ine ndine Yosefe mbale wanu, ine ndemwe munandigulitsa ndilowe mu Ejipito.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, Muyandikiretu kwa ine; nayandikira. Ndipo iye anati, Ine ndine Yosefe mbale wanu, ine ndemwe munandigulitsa ndilowe m'Ejipito.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Yosefe adaŵauza kuti, “Chonde senderani pafupi.” Onse atabwera pafupi, Yosefe adati, “Ine ndine mbale wanu uja Yosefe, amene mudamgulitsa ku Ejipito.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!

Onani mutuwo



Genesis 45:4
5 Mawu Ofanana  

Ndipo anapita pamenepo Amidiyani a malonda: ndipo anamtulutsa namkweza Yosefe m'dzenjemo, namgulitsa kwa Aismaele ndi masekeli a siliva makumi awiri; ndipo ananka naye Yosefe ku Ejipito.


Ndiponso abale ake anamuka namgwadira pamaso pake; nati, Taonani, ife ndife akapolo anu.


Koma pomwepo Yesu analankhula nao, nati, Limbani mtima; ndine; musaope.


Ndipo makolo aakuluwa podukidwa naye Yosefe, anamgulitsa amuke naye ku Ejipito; ndipo Mulungu anali naye,


Koma anati, Ndinu yani Mbuye? Ndipo anati, Ndine Yesu amene umlondalonda;