Genesis 42:11 - Buku Lopatulika Tonse tili ana aamuna a munthu mmodzi; tili oona, akapolo anu, sitili ozonda. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Tonse tili ana amuna a munthu mmodzi; tili oona, akapolo anu, sitili ozonda. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Tonsefe tili pachibale. Sindife azondi, mbuyathu, koma ndife anthu okhulupirika ndithu.” Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.” |
Tumizani mmodzi wa inu akatenge, adze naye mphwanu: ndipo inu mudzamangidwa kuti mau anu ayesedwe, ngati zoona zili mwa inu: penatu, pali moyo wa Farao, muli ozonda ndithu.
ngati muli oona, mmodzi wa abale anu amangidwe m'kaidi momwemo; mukani inu, mupite naye tirigu wa njala ya mabanja anu;
Ndipo iwo anati, Munthuyo anafunsitsa za ife, ndi za abale athu, kuti, Atate wanu alipo? Kodi muli ndi mphwanu? Ndipo tinamfotokozera iye monga mwa mau amenewo: ngati tinadziwa kuti iye adzati, Idzani naye mphwanu?
Iye wolankhula zochokera kwa iye yekha afuna ulemu wa mwini yekha. Iye wakufuna ulemu wa Iye amene anamtuma, yemweyu ali woona, ndipo mwa Iye mulibe chosalungama.
koma m'zonse tidzitsimikizira ife tokha monga atumiki a Mulungu, m'kupirira kwambiri, m'zisautso, m'zikakamizo, m'zopsinja,