Ndipo Isaki anabzala m'dzikomo, nalandira za makumi khumi chaka chimenecho; ndipo Yehova anamdalitsa iye.
Genesis 41:47 - Buku Lopatulika Ndipo zaka zisanu ndi ziwiri zakuchuluka dzinthu nthaka inabala zambirimbiri. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo zaka zisanu ndi ziwiri zakuchuluka dzinthu nthaka inabala zambirimbiri. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Pa zaka zija za dzinthu dzambiri, m'dziko lonse munali chakudya chochuluka kwambiri. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mʼzaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zambiri zija, anthu mʼdzikomo anakolola zochuluka. |
Ndipo Isaki anabzala m'dzikomo, nalandira za makumi khumi chaka chimenecho; ndipo Yehova anamdalitsa iye.
Taonani, zidzafika zaka zisanu ndi ziwiri zakuchuluka chakudya m'dziko lonse la Ejipito;
Ndipo Yosefe anali wa zaka makumi atatu pamene iye anaima pamaso pa Farao mfumu ya Aejipito. Ndipo Yosefe anatuluka pamaso pa Farao, napitapita padziko lonse la Ejipito.
Ndipo anasonkhanitsa chakudya chonse cha zaka zisanu ndi ziwiri chimene chinali m'dziko la Ejipito, nasunga chakudyacho m'mizinda; chakudya cha m'minda, yozinga mizinda yonse, anachisunga m'menemo.
M'dzikomo mudzakhala dzinthu dzochuluka pamwamba pa mapiri; zipatso zake zidzati waa, ngati za ku Lebanoni, ndipo iwo a m'mizinda adzaphuka ngati msipu wapansi.