Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 39:10 - Buku Lopatulika

Ndipo pali pakunenanena ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, iye sanamvere mkazi kugona naye kapena kukhala naye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pali pakunenanena ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, iye sanamvere mkazi kugona naye kapena kukhala naye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngakhale mkazi uja ankalankhula mau ameneŵa kwa Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefeyo sankamvako mpang'ono pomwe, ndipo sankalola kuchita naye zoipa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.

Onani mutuwo



Genesis 39:10
21 Mawu Ofanana  

Ndipo panali, nthawi yomweyo, iye analowa m'nyumba kuti agwire ntchito yake; ndipo munalibe amuna a m'nyumba m'katimo.


Koma iye anakana, nati kwa mkazi wa mbuyake, Taonani, mbuyanga sadziwa chimene chili ndi ine m'nyumbamu, ndipo anaika zake zonse m'manja anga;


mulibe wina m'nyumba wamkulu ndine; ndipo sanandikanize ine kanthu, koma iwe, chifukwa kuti uli mkazi wake: nanga ndikachita choipa chachikulu ichi bwanji ndi kuchimwira Mulungu?


Mwananga, usayende nao m'njira; letsa phazi lako ku mayendedwe ao;


Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere, kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake;


M'kamwa mwa mkazi wachiwerewere muli dzenje lakuya; yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.


Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya; ndipo mkazi wachiwerewere ndiye mbuna yopapatiza.


Pakuti abisalira ngati wachifwamba, nachulukitsa anthu a chiwembu.


Pakuti milomo ya mkazi wachiwerewere ikukha uchi; m'kamwa mwake muti see koposa mafuta.


Siyanitsa njira yako kutali kwa iyeyo, osayandikira ku khomo la nyumba yake;


Ndipo anagwira mnyamatayo, nampsompsona; nati kwa iye ndi nkhope yachipongwe,


Kuti zikutchinjirizire kwa mkazi wachiwerewere, kwa mlendo wamkazi wosyasyalika ndi mau ake.


Ukhala pa khomo la nyumba yake, pampando pa misanje ya m'mudzi,


wachibwana ndani? Apatukire kuno. Ati kwa yense wopanda nzeru,


Musanyengedwe; mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma.


Thawani dama. Tchimo lililonse munthu akalichita lili kunja kwa thupi; koma wachiwerewere achimwira thupi lake la iye yekha.


Mupewe maonekedwe onse a choipa.


Chifukwa chake nditi akwatiwe amasiye aang'ono, nabale ana, naweruzire nyumba, osapatsa chifukwa kwa mdaniyo chakulalatira;


Koma thawa zilakolako za unyamata, nutsate chilungamo, chikhulupiriro, chikondi, mtendere, pamodzi ndi iwo akuitana pa Ambuye ndi mitima yoyera.


Okondedwa, ndikudandaulirani ngati alendo ndi ogonera mudzikanize zilakolako za thupi zimene zichita nkhondo pa moyo;