Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 27:9 - Buku Lopatulika

Pitatu kubusa, ukanditengere ine kumeneko tiana tiwiri tabwino tambuzi; ndikonzere nato chakudya chokolera cha atate wako chonga chomwe achikonda:

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pitatu kubusa, ukanditengere ine kumeneko tiana tiwiri tabwino tambuzi; ndikonzere nato chakudya chokolera cha atate wako chonga chomwe achikonda:

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pita ku khola, ukanditengere timbuzi tiŵiri tonenepa bwino, kuti ndiphike, ndi kukonza chakudya chimene bambo wako amachikonda.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pita ku khola, ukatenge ana ambuzi abwino awiri, kuti ndikonzere abambo ako chakudya chokoma monga amakondera.

Onani mutuwo



Genesis 27:9
6 Mawu Ofanana  

ndipo udzapita nacho kwa atate wako, kuti adye, ndi kukudalitsa iwe asanafe.


Ndipo anamuka nakatenga nadza nato kwa amake; amake ndipo anakonza chakudya chokolera chonga chimene anachikonda atate wake.


nundikonzere ine chakudya chokolera chonga chomwe ndichikonda ine, nudze nacho kwa ine kuti ndidzadye; kuti moyo wanga ukadalitse iwe ndisanafe.


Tsopanotu mwana wanga, tamvera mau anga monga momwe nditi ndikuuze iwe.


Ndipo Manowa anati kwa mthenga wa Yehova, Tiloleni tikuchedwetseni kuti tikukonzereni mwanawambuzi.


Ndipo Yese anatenga bulu namsenza mkate, ndi thumba la vinyo, ndi mwanawambuzi, nazitumiza kwa Saulo ndi Davide mwana wake.