Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 39:18 - Buku Lopatulika

Ndi nsonga zake ziwiri zina za maunyolo awiri opotawo anazimanga pa zoikamo ziwiri, nazimanga pa zapamapewa za efodi, m'tsogolo mwake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndi nsonga zake ziwiri zina za maunyolo awiri opotawo anazimanga pa zoikamo ziwiri, nazimanga pa zapamapewa za efodi, m'tsogolo mwake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

ndi kulumikiza nsonga ziŵiri zina za zingwezo m'zoikamo zake ziŵiri zija. Motero adazilumikiza patsogolo pa tizikwewo tam'mapewa ta chovala cha efodi chija.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo mbali ina ya timaunyoloto anamangirira pa zoyikapo zake ziwiri zija, ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.

Onani mutuwo



Eksodo 39:18
6 Mawu Ofanana  

Uloche miyala iwiriyo ndi maina a ana a Israele, monga mwa ntchito ya wolocha miyala, monga malembedwe a chosindikizira, uipange igwirike ndi zoikamo zagolide.


ndi maunyolo awiri a golide woona; uwapote ngati zingwe, ntchito yopota; numange maunyolo opotawo pazoikamo.


Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zake ziwiri, kuti amangike nazo.


Ndipo anamanga maunyolo awiri opota agolide pa mphete ziwiri pansonga za chapachifuwa.


Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolide, naziika pansonga ziwiri za chapachifuwa, m'mphepete mwake m'katimo, pa mbali ya kuefodi.


Masaya ako akongola ndi nkhata zatsitsi, ndi khosi lako ndi zinganga za mkanda wonyezimira.