Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 30:19 - Buku Lopatulika

Ndipo Aroni ndi ana ake aamuna azisambiramo manja ao ndi mapazi ao;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Aroni ndi ana ake amuna azisambiramo manja ao ndi mapazi ao;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Aroni ndi ana ake azisamba m'manja ndi kutsuka mapazi ao ndi madzi amenewo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aaroni ndi ana ake azisamba mʼmanja ndi kutsuka mapazi awo ndi madzi amenewo.

Onani mutuwo



Eksodo 30:19
12 Mawu Ofanana  

Ndidzasamba manja anga mosalakwa; kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova;


Ndipo ubwere nao Aroni ndi ana ake aamuna ku khomo la chihema chokomanako, ndi kuwasambitsa m'madzi.


pakulowa iwo m'chihema chokomanako asambe ndi madzi, kuti angafe; kapena poyandikiza guwa la nsembe kutumikirako, kufukiza nsembe yamoto ya Yehova;


Chokani inu, chokani inu, tulukani ku Babiloni; musakhudze kanthu kodetsa; tulukani pakati pake, khalani okonzeka, inu amene munyamula zotengera za Yehova.


Ndipo Mose anabwera nao Aroni ndi ana ake, nawasambitsa ndi madzi.


zosati zochokera m'ntchito za m'chilungamo, zimene tidazichita ife, komatu monga mwa chifundo chake anatipulumutsa ife, mwa kutsuka kwa kubadwanso ndi makonzedwe a Mzimu Woyera,


tiyandikire ndi mtima woona, m'chikhulupiriro chokwanira, ndi mitima yathu yowazidwa kuichotsera chikumbumtima choipa, ndi matupi athu osambitsidwa ndi madzi oyera;


Popeza akhala zoikika za thupi zokha (ndi zakudya, ndi zakumwa, ndi masambidwe osiyanasiyana), oikidwa kufikira nthawi yakukonzanso.