Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 28:25 - Buku Lopatulika

Koma nsonga zake ziwiri za maunyolo opotawo uzimange ku zoikamo ziwiri, ndi kuziika pa zapamapewa ziwiri za efodi, m'tsogolo mwake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma nsonga zake ziwiri za maunyolo opotawo uzimange ku zoikamo ziwiri, ndi kuziika pa zapamapewa ziwiri za efodi, m'tsogolo mwake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo nsonga zake zina ziŵiri za zingwezo uzimange ku zoikamo zake zija.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.

Onani mutuwo



Eksodo 28:25
7 Mawu Ofanana  

Uloche miyala iwiriyo ndi maina a ana a Israele, monga mwa ntchito ya wolocha miyala, monga malembedwe a chosindikizira, uipange igwirike ndi zoikamo zagolide.


ndi maunyolo awiri a golide woona; uwapote ngati zingwe, ntchito yopota; numange maunyolo opotawo pazoikamo.


Numange maunyolo awiri opota agolide ku mphete ziwirizo pansonga pake pa chapachifuwa.


Ndipo upange mphete ziwiri zagolide, ndi kuzimanga pansonga zake ziwiri za chapachifuwa, m'mphepete mwake, m'katimo ku mbali ya kuefodi.


Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zake ziwiri, kuti amangike nazo.


Ndipo anapangira pachapachifuwa maunyolo ngati zingwe, ntchito yopota ya golide woona.


Anapangira efodi zapamapewa zolumikizana; pansonga ziwirizo anamlumikiza.