Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 39:15 - Buku Lopatulika

15 Ndipo anapangira pachapachifuwa maunyolo ngati zingwe, ntchito yopota ya golide woona.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

15 Ndipo anapangira pachapachifuwa maunyolo ngati zingwe, ntchito yopota ya golide woona.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

15 Adapanga timaunyolo ta chovala chapachifuwa ta golide wabwino kwambiri, topota mwaluso ngati maukufu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

15 Anapanga timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 39:15
9 Mawu Ofanana  

M'nyumba yaikulu tsono anatchinga ndi mitengo yamlombwa, imene anaikuta ndi golide wabwino, nalembapo ngati migwalangwa ndi maunyolo.


ndi maunyolo awiri a golide woona; uwapote ngati zingwe, ntchito yopota; numange maunyolo opotawo pazoikamo.


Ndipo miyalayi inakhala monga mwa maina a ana a Israele, khumi ndi awiri, monga mwa maina ao; ngati malochedwe a chosindikizira, yonse monga mwa maina ake, kwa mafuko khumi ndi awiriwo.


Anapanganso zoikamo ziwiri zagolide, ndi mphete ziwiri zagolide; naika mphete ziwirizo pansonga ziwiri za chapachifuwa.


Masaya ako akongola ndi nkhata zatsitsi, ndi khosi lako ndi zinganga za mkanda wonyezimira.


Ndipo Ine ndizipatsa moyo wosatha; ndipo sizidzaonongeka kunthawi yonse, ndipo palibe munthu adzazikwatula m'dzanja langa.


Pamene ndinakhala nao, Ine ndinalikuwasunga iwo m'dzina lanu amene mwandipatsa Ine; ndipo ndinawasunga, ndipo sanatayike mmodzi yense wa iwo, koma mwana wa chitayiko, kuti lembo likwaniridwe.


amene musungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mwa chikhulupiriro, kufikira chipulumutso chokonzeka kukavumbulutsidwa nthawi yotsiriza.


Yuda, kapolo wa Yesu Khristu, ndi mbale wa Yakobo, kwa iwo oitanidwa, okondedwa mwa Mulungu Atate, ndi osungidwa ndi Yesu Khristu:


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa