Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 20:1 - Buku Lopatulika

Ndipo Mulungu ananena mau onse amenewa, nati,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Mulungu ananena mau onse amenewa, nati:

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Mulungu adalankhula mau onseŵa, adati,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:

Onani mutuwo



Eksodo 20:1
11 Mawu Ofanana  

Munatsikiranso paphiri la Sinai, nimunalankhula nao mochokera mu Mwamba, ndipo munawapatsa maweruzo oyenera, ndi chilamulo choona, malemba, ndi malamulo okoma;


Pamenepo Mose anawatsikira anthu, nanena nao.


Ine ndine Yehova Mulungu wako, amene ndinatulutsa iwe ku dziko la Ejipito, kunyumba ya ukapolo.


Uyu ndiye amene anali mu Mpingo m'chipululu pamodzi ndi mngelo wakulankhula naye m'phiri la Sinai, ndi makolo athu: amene analandira maneno amoyo akutipatsa ife;


inu amene munalandira chilamulo monga chidaikidwa ndi angelo, ndipo simunachisunge.


Ndipo analembera pamagome, monga mwa malembedwe oyamba, mau khumiwo, amene Yehova adanena ndi inu m'phirimo, ali pakati pa moto, tsiku la kusonkhanako; ndipo Yehova anandipatsa awa.


Kodi pali mtundu wa anthu udamva mau a mulungu wina akunena pakati pa moto, monga mudamva inu, ndi kukhala ndi moyo?


Anakumvetsani mau ake kuchokera kumwamba, kuti akuphunzitseni; ndipo padziko lapansi anakuonetsani moto wake waukulu; nimunamva mau ake pakati pa moto.


Yehova ananena mau awa kwa msonkhano wanu wonse, m'phirimo ali pakati pa moto, pamtambo, pamdima bii, ndi mau aakulu; osaonjezapo kanthu. Ndipo anawalembera pa magome awiri amiyala, nandipatsa awa.


Yehova ananena ndi inu popenyana maso m'phirimo, ali pakati pa moto,


Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa m'dziko la Ejipito, m'nyumba ya ukapolo.