Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 18:15 - Buku Lopatulika

Ndipo Mose anati kwa mpongozi wake, Chifukwa anthu amadza kwa ine kudzafunsira Mulungu;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Mose anati kwa mpongozi wake, Chifukwa anthu amadza kwa ine kudzafunsira Mulungu;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mose adayankha kuti, “Ndiyenera kuchita zimenezi chifukwa choti anthu amabwera kwa ine, kuti amve zimene Mulungu afuna.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.

Onani mutuwo



Eksodo 18:15
9 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene mpongozi wake wa Mose anaona zonsezi iye anawachitira anthu, anati, Chinthu ichi nchiyani uwachitira anthuchi? Umakhala pa wekha bwanji, ndi anthu onse amakhala chilili pamaso pako kuyambira m'mawa kufikira madzulo?


Ndipo anayamba wamsunga, popeza sichinanenedwe choyenera kumchitira iye.


Ndipo Mose anapita nao mlandu wao pamaso pa Yehova.


Pamenepo panali amuna, anadetsedwa ndi mtembo wa munthu, ndipo sanakhoze kuchita Paska tsiku lomwelo; m'mwemo anafika pamaso pa Mose ndi pamaso pa Aroni tsiku lomwelo;


Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve chouza Yehova za inu.


Ndipo atafa Yoswa, ana a Israele anafunsira kwa Yehova ndi kuti, Adzayamba ndani kutikwerera pa Akanani kuwathira nkhondo?