Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 9:8 - Buku Lopatulika

8 Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve chouza Yehova za inu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve chouza Yehova za inu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Mose adayankha kuti, “Dikirani kuti ndimve zimene Chauta alamule za inu.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”

Onani mutuwo Koperani




Numeri 9:8
19 Mawu Ofanana  

Si kwanu kuchita nkhondo kuno ai; chilimikani, imani, nimupenye chipulumutso cha Yehova pa inu Yuda ndi Yerusalemu; musaope, kapena kutenga nkhawa; mawa muwatulukire, popeza Yehova ali ndi inu.


Chinsinsi cha Yehova chili kwa iwo akumuopa Iye; ndipo adzawadziwitsa pangano lake.


Ndidzamva cholankhula Mulungu Yehova; pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ake, ndi okondedwa ake; koma asabwererenso kuchita zopusa.


Ndipo Mose ananena ndi anthu, Musaope, chilimikani, ndipo penyani chipulumutso cha Yehova, chimene adzakuchitirani lero; pakuti Aejipito mwawaona lerowa, simudzawaonanso konse.


Ndipo Mose anati kwa mpongozi wake, Chifukwa anthu amadza kwa ine kudzafunsira Mulungu;


Ndipo ukanene nao mau anga, ngakhale akamva kapena akaleka kumva; pakuti iwo ndiwo opanduka.


Wobadwa ndi munthu iwe, ndakuika ukhale mlonda wa nyumba ya Israele, m'mwemo mvera mau otuluka m'kamwa mwanga, nundichenjezere iwo.


Ndipo anamsunga m'kaidi, kuti awafotokozere m'mene anenere Yehova.


Ndipo anayamba wamsunga, popeza sichinanenedwe choyenera kumchitira iye.


Ndipo Mose anapita nao mlandu wao pamaso pa Yehova.


nanena naye amunawa, Tadetsedwa ife ndi mtembo wa munthu; atiletseranji, kuti tisabwere nacho chopereka cha Yehova pa nyengo yake yoikidwa, pakati pa ana a Israele?


Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,


chifukwa mau amene munandipatsa Ine ndinapatsa iwo; ndipo analandira, nazindikira koona kuti ndinatuluka kwa Inu, ndipo anakhulupirira kuti Inu munandituma Ine.


Ngati munthu aliyense afuna kuchita chifuniro chake, adzazindikira za chiphunzitsocho, ngati chichokera kwa Mulungu, kapena ndilankhula zochokera kwa Ine ndekha.


Pakuti sindinakubisirani pakukulalikirani uphungu wonse wa Mulungu.


Pakuti ine ndinalandira kwa Ambuye, chimenenso ndinapereka kwa inu, kuti Ambuye Yesu usiku uja anaperekedwa, anatenga mkate;


Pakuti sindidziwa kanthu kakundipalamulitsa; koma m'menemo sindiyesedwa wolungama; koma wondiweruza ine ndiye Ambuye.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa