Eksodo 14:5 - Buku Lopatulika Ndipo anauza mfumu ya Aejipito kuti anthu adathawa; ndi mtima wa Farao ndi wa anyamata ake inasandulikira anthuwo, ndipo anati, Ichi nchiyani tachita, kuti talola Israele amuke osatigwiriranso ntchito? Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo anauza mfumu ya Aejipito kuti anthu adathawa; ndi mtima wa Farao ndi wa anyamata ake inasandulikira anthuwo, ndipo anati, Ichi nchiyani tachita, kuti talola Israele amuke osatigwiriranso ntchito? Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Atamva kuti anthu athaŵa, Farao, mfumu ya ku Ejipito, pamodzi ndi nduna zake zonse, adasintha maganizo pa za Aisraelewo. Adati, “Kodi ife tachitapo chiyani pamenepa? Talola Aisraele kuti athaŵe ndi kuleka kutitumikira.” Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Farao, mfumu ya Igupto atamva kuti anthu aja athawa, iye pamodzi ndi nduna zake anasintha maganizo awo pa Israeli ndipo anati, “Ife tachita chiyani? Tawalola Aisraeli kuti apite ndi kuleka kutitumikira?” |
Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ake, kuti achite monyenga ndi atumiki ake.
Ndipo Aejipito anaumiriza anthuwo, nafulumira kuwatulutsa m'dziko; pakuti anati, Tili akufa tonse.
Ndipo ndidzalimbitsa mtima wake wa Farao kuti awalondole; ndipo ndidzalemekezedwa pa Farao ndi pa nkhondo yake yonse; pamenepo Aejipito adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndipo anachita chomwecho.
Mdani anati, Ndiwalondola, ndiwapeza, ndidzagawa zofunkha; ndidzakhuta nao mtima; ndidzasolola lupanga langa, dzanja langa lidzawaononga.