Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 14:5 - Buku Lopatulika

Ndipo anauza mfumu ya Aejipito kuti anthu adathawa; ndi mtima wa Farao ndi wa anyamata ake inasandulikira anthuwo, ndipo anati, Ichi nchiyani tachita, kuti talola Israele amuke osatigwiriranso ntchito?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anauza mfumu ya Aejipito kuti anthu adathawa; ndi mtima wa Farao ndi wa anyamata ake inasandulikira anthuwo, ndipo anati, Ichi nchiyani tachita, kuti talola Israele amuke osatigwiriranso ntchito?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Atamva kuti anthu athaŵa, Farao, mfumu ya ku Ejipito, pamodzi ndi nduna zake zonse, adasintha maganizo pa za Aisraelewo. Adati, “Kodi ife tachitapo chiyani pamenepa? Talola Aisraele kuti athaŵe ndi kuleka kutitumikira.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Farao, mfumu ya Igupto atamva kuti anthu aja athawa, iye pamodzi ndi nduna zake anasintha maganizo awo pa Israeli ndipo anati, “Ife tachita chiyani? Tawalola Aisraeli kuti apite ndi kuleka kutitumikira?”

Onani mutuwo



Eksodo 14:5
9 Mawu Ofanana  

Tsiku lachitatu anamuuza Labani kuti Yakobo wathawa.


Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ake, kuti achite monyenga ndi atumiki ake.


Ndipo Aejipito anaumiriza anthuwo, nafulumira kuwatulutsa m'dziko; pakuti anati, Tili akufa tonse.


Ndipo ndidzalimbitsa mtima wake wa Farao kuti awalondole; ndipo ndidzalemekezedwa pa Farao ndi pa nkhondo yake yonse; pamenepo Aejipito adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndipo anachita chomwecho.


Ndipo anamanga galeta lake, napita nao anthu ake;


Mdani anati, Ndiwalondola, ndiwapeza, ndidzagawa zofunkha; ndidzakhuta nao mtima; ndidzasolola lupanga langa, dzanja langa lidzawaononga.