Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Afilipi 3:16 - Buku Lopatulika

chokhachi, kumene tidafikirako, mayendedwe athu alinganeko.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

chokhachi, kumene tidafikirako, mayendedwe athu alinganeko.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ngakhale zitani, tisatayepo kanthu pa zoona zimene takhala tikuzikhulupirira mpaka tsopano.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.

Onani mutuwo



Afilipi 3:16
14 Mawu Ofanana  

Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake. Musasamalire zinthu zazikulu, koma phatikanani nao odzichepetsa. Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.


Ndipo Mulungu wa chipiriro ndi wa chitonthozo apatse inu kuti mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake, monga mwa Khristu Yesu;


Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere choonadi?


Ndipo onse amene atsata chilangizo ichi, mtendere ndi chifundo zikhale pa iwo, ndi pa Israele wa Mulungu.


Chokhachi, mayendedwe anu ayenere Uthenga Wabwino wa Khristu: kuti, ndingakhale nditi ndilinkudza ndi kuona inu, ndingakhale nditi ndili kwina, ndikamva za kwa inu, kuti muchilimika mu mzimu umodzi, ndi kugwirira pamodzi ndi moyo umodzi chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino;


kwaniritsani chimwemwe changa, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala nacho chikondi chomwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi;


Ndidandaulira Yuwodiya, ndidandaulira Sintike, alingirire ndi mtima umodzi mwa Ambuye.


Chifukwa chake monga momwe munalandira Khristu Yesu Ambuye, muyende mwa Iye,


Chitani khama m'kupemphera, nimudikire momwemo ndi chiyamiko;


Chifukwa chake kumbukira umo unalandira nunamvamo; nusunge nulape. Ukapanda kudikira tsono, ndidzafika ngati mbala, ndipo sudzazindikira nthawi yake ndidzadza pa iwe.