Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 22:45 - Buku Lopatulika

Alendo adzandigonjera ine, pakumva za ine, adzandimvera pomwepo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Alendo adzandigonjera ine, pakumva za ine, adzandimvera pomwepo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu a maiko ena adabwera kwa ine kudzapemba; atangomva mau anga oyamba adandimvera.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.

Onani mutuwo



2 Samueli 22:45
8 Mawu Ofanana  

Nenani kwa Mulungu, Ha, ntchito zanu nzoopsa nanga! Chifukwa cha mphamvu yanu yaikulu adani anu adzagonjera Inu.


Akumuda Yehova akadamgonjera mungakhale monyenga, koma nyengo yao ikadakhala yosatha.


Mlendo amene wadziphatika yekha kwa Yehova asanene, kuti, Yehova adzandilekanitsa ndithu ndi anthu ake; pena mfule asanene, Taonani ine ndili mtengo wouma.


Alendonso amene adziphatika okha kwa Yehova, kuti amtumikire Iye, ndi kukonda dzina la Yehova, akhale atumiki ake, yense amene asunga sabata osaliipitsa, nagwira zolimba chipangano changa;


Ndipo Simoni mwini wake anakhulupiriranso: ndipo m'mene anabatizidwa, anakhalira ndi Filipo; ndipo pakuona zizindikiro ndi mphamvu zazikulu zilikuchitika, anadabwa.


Wodala iwe, Israele; akunga iwe ndani, mtundu wa anthu opulumutsidwa ndi Yehova, ndiye chikopa cha thandizo lako, Iye amene akhala lupanga la ukulu wako! Ndi adani ako adzakugonjera; ndipo udzaponda pa misanje yao.