Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 18:15 - Buku Lopatulika

Ndipo anyamata khumi onyamula zida zake za Yowabu anamzungulira Abisalomu namkantha namupha.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anyamata khumi onyamula zida zake za Yowabu anamzungulira Abisalomu namkantha namupha.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pomwepo ankhondo khumi onyamula zida zankhondo za Yowabu, adazinga Abisalomu, namkantha mpaka kumupha.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.

Onani mutuwo



2 Samueli 18:15
9 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake tsono lupanga silidzachoka pa nyumba yako nthawi zonse, popeza unandipeputsa Ine, nudzitengera mkazi wa Uriya Muhiti akhale mkazi wako.


Pomwepo Yowabu anati, Sindiyenera kuchedwa nawe. Natenga mikondo itatu nagwaza nayo mtima wa Abisalomu alikukhala wamoyo pakati pa mtengowo.


Ndipo Yowabu analiza lipenga, ndipo anthu anabwerera naleka kupirikitsa Aisraele; pakuti Yowabu analetsa anthuwo.


Ndipo mfumu Davide anatumiza kwa Zadoki ndi Abiyatara ansembewo, nati, Mulankhule nao akulu a Yuda, kuti, Mukhale bwanji am'mbuyo kubwera nayo mfumu kunyumba yake? Pakuti mau a Aisraele onse anafika kwa mfumu akuti abwere nayo kunyumba yake.


kuti kufuula kokondwera kwa woipa sikukhalira kutha, ndi chimwemwe cha wonyoza Mulungu chikhala kamphindi?


Ndapenya woipa, alikuopsa, natasa monga mtengo wauwisi wanzika.


Woipa amafuna kupanduka kokha; koma adzamtumizira mthenga wankhanza.


Wopalamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje; asamuletse.


Wokumba mbuna adzagwamo; ndipo woboola mpanda njoka idzamluma.