Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 134 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 134

Afulumizidwa anthu kulemekeza Yehova
Nyimbo yokwerera.

1 Taonani, lemekezani Yehova, atumiki a Yehova inu nonse, akuimirira m'nyumba ya Yehova usiku.

2 Kwezani manja anu kumalo oyera, nimulemekeze Yehova.

3 Yehova, ali mu Ziyoni, akudalitseni; ndiye amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi