Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 131 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 131

Kudzichepetsa kwa Davide pakupemphera
Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Yehova, mtima wanga sunadzikuze ndi maso anga sanakwezeke; ndipo sindinatsate zazikulu, kapena zodabwitsa zondiposa.

2 Indedi, ndinalinganiza ndi kutontholetsa moyo wanga; ngati mwana womletsa kuyamwa amake, moyo wanga ndili nao ngati mwana womletsa kuyamwa.

3 Israele, uyembekezere Yehova, kuyambira tsopano kufikira kosatha.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi