Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mlaliki 11:1 - Buku Lopatulika

1 Ponya zakudya zako pamadzi; udzazipeza popita masiku ambiri.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Ponya zakudya zako pamadzi; udzazipeza popita masiku ambiri.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Ndalama zako uziike pa malonda okagulitsa kutsidya kwa nyanja, ndipo udzapeza phindu patapita masiku ambiri.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.

Onani mutuwo Koperani




Mlaliki 11:1
21 Mawu Ofanana  

ndi uchi ndi mafuta, ndi nkhosa, ndi mase a ng'ombe, kuti adye Davide, ndi anthu amene anali naye; pakuti anati, Anthu ali ndi njala, olema, ndi aludzu m'chipululumo.


Woipa alandira malipiro onyenga; koma wofesa chilungamo aonadi mphotho.


Wochitira waumphawi chifundo abwereka Yehova; adzambwezera chokoma chakecho.


Mwini diso lamataya adzadala; pakuti apatsa osauka zakudya zake.


Mamawa fesa mbeu zako, madzulonso osapumitsa dzanja lako; pakuti sudziwa ziti zidzalola bwino ngakhale izizi, ngakhale izozo, kaya zonse ziwiri zidzakhala bwino.


mphindi yakufunafuna ndi mphindi yakumwazika; mphindi yakusunga ndi mphindi yakutaya;


Odala muli inu, amene mubzala m'mbali mwa madzi monse, amene muyendetsa mapazi a ng'ombe ndi bulu.


Koma mfulu aganizira zaufulu, nakhazikika m'zaufulu zomwe.


Chaka chachisanu muzidya zipatso zake, kuti zobala zake zikuchulukireni inu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.


Ndipo ngati nyumbayo ili yoyenera, mtendere wanu udze pa iyo, koma ngati siili yoyenera, mtendere wanu ubwerere kwa inu.


Ndipo aliyense amene adzamwetsa mmodzi wa ang'ono awa chikho chokha cha madzi ozizira, pa dzina la wophunzira, indetu ndinena kwa inu, iye sadzataya mphotho yake.


Chimodzimodzi uyo wa awiriwo, anapindulapo ena awiri.


Ndipo Mfumuyo idzayankha nidzati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Chifukwa munachitira ichi mmodzi wa abale anga, ngakhale ang'onong'ono awa, munandichitira ichi Ine.


ndipo udzakhala wodala; chifukwa iwo alibe chakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa olungama.


Koma nditi ichi, kuti iye wakufesa mouma manja, mouma manjanso adzatuta. Ndipo iye wakufesa moolowa manja, moolowa manjanso adzatuta.


pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala ntchito yanu, ndi chikondicho mudachionetsera kudzina lake, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa