Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 72:12 - Buku Lopatulika

12 Pakuti adzapulumutsa waumphawi wofuulayo; ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

12 Pakuti adzapulumutsa waumphawi wofuulayo; ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

12 Ndithu iyo idzalanditsa anthu osoŵa amene amaiitana, idzapulumutsa anthu osauka ndiponso opanda woŵathandiza.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 72:12
19 Mawu Ofanana  

Pakuti mfumu idzamvera ndi kupulumutsa mdzakazi wake m'dzanja la munthu wakufuna kundiononga ine pamodzi ndi mwana wanga, kutichotsa ku cholowa cha Mulungu.


Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakufuula; mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.


Apulumutsa wozunzika mwa kuzunzika kwake, nawatsegulira m'khutu mwao mwa kupsinjika kwao.


Yehova, mwamva chikhumbo cha ozunzika, mudzakhazikitsa mtima wao, mudzatchereza khutu lanu;


anasamalira pemphero la iwo akusowa konse, osapepula pemphero lao.


kuti amve kubuula kwa wandende; namasule ana a imfa.


Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula, ndipo adzamva mau anga.


Adzaweruza ozunzika a mwa anthu, adzapulumutsa ana aumphawi, nadzaphwanya wosautsa.


Wolungama asamalira mlandu wa osauka; koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.


Ndinabweranso tsono ndi kupenyera nsautso zonse zimachitidwa kunja kuno; ndipo taona, misozi ya otsenderezedwa, koma analibe wakuwatonthoza; ndipo akuwatsendereza anali ndi mphamvu koma iwowa analibe wakuwatonthoza.


Wosauka ndi wosowa afuna madzi, ndipo palibe, ndi lilime lao lilephera, chifukwa cha ludzu; Ine Yehova ndidzawayankha, Ine Mulungu wa Israele sindidzawasiya.


Mzimu wa Ambuye uli pa Ine, chifukwa chake Iye anandidzoza Ine ndiuze anthu osauka Uthenga Wabwino: anandituma Ine kulalikira am'nsinga mamasulidwe, ndi akhungu kuti apenyanso, kutulutsa ndi ufulu ophwanyika,


Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Mukani, muuze Yohane zimene mwaziona, nimwazimva; anthu akhungu alandira kuona kwao, opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, ogontha akumva, akufa aukitsidwa, kwa aumphawi ulalikidwa Uthenga Wabwino.


Pakuti mudziwa chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti, chifukwa cha inu anakhala wosauka, angakhale anali wolemera, kuti inu ndi kusauka kwake mukakhale olemera.


kuchokera komweko akhoza kupulumutsa konsekonse iwo akuyandikira kwa Mulungu mwa Iye, popeza ali nao moyo wake chikhalire wa kuwapembedzera iwo.


Ndipo yense wosautsidwa, ndi yense wa ngongole, ndi yense wowawidwa mtima, anaunjikana kwa iye; iye nakhala mtsogoleri wao; ndipo anali nao anthu ngati mazana anai.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa