Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 60:3 - Buku Lopatulika

3 Mwaonetsa anthu anu zowawa, mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Mwaonetsa anthu anu zowawa, mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Inu mwalola anthu anu kuti aone mavuto aakulu. Mwatipatsa vinyo wachilango kuti timwe, ndipo tikudzandira naye.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 60:3
16 Mawu Ofanana  

Ndipo tsono, Mulungu wathu, ndinu Mulungu wamkulu, ndi wamphamvu, ndi woopsa, wakusunga pangano ndi chifundo, asachepe pamaso panu mavuto athu onse amene anatigwera ife, ndi mafumu athu, akulu athu, ndi ansembe athu, ndi aneneri athu, ndi makolo athu, ndi anthu anu onse, kuyambira masiku a mafumu a Asiriya, mpaka lero lino.


Inu, amene munationetsa nsautso zambiri ndi zoipa, mudzatipatsanso moyo, ndi kutitenganso munsi mwa dziko.


Pakuti m'dzanja la Yehova muli chikho; ndi vinyo wake achita thovu; chidzala ndi zosakanizira, ndipo atsanulako. Indedi, oipa onse a padziko lapansi adzamwa nadzagugudiza nsenga zake.


Yehova, Mulungu wa makamu, mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?


Mudatenga mpesa kuchokera ku Ejipito, munapirikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.


Kodi mudzatikwiyira nthawi zonse? Kodi mudzakhala chikwiyire mibadwomibadwo?


Munakaniza chipangano cha mtumiki wanu; munaipsa korona wake ndi kumponya pansi.


Galamuka, galamuka, imirira Yerusalemu amene unamwa m'dzanja la Yehova chikho cha ukali wake; iwe wamwa mbale ya chikho chonjenjemeretsa ndi kuchigugudiza.


atero Ambuye ako Yehova, ndi Mulungu wako amene anena mlandu wa anthu ake, Taona, ndachotsa m'dzanja mwako chikho chonjenjemeretsa, ngakhale mbale ya chikho cha ukali wanga; iwe sudzamwa icho kawirinso.


Pakuti Yehova, Mulungu wa Israele, atero kwa ine, Tenga chikho cha vinyo wa ukaliwu padzanja langa, ndi kumwetsa mitundu yonse, imene ndikutumizirako.


kondwera nusangalale, mwana wamkazi wa Edomu, wokhala m'dziko la Uzi; chikho chidzapita ngakhale mwa iwenso; udzaledzera ndi kuvula zako.


Ndipo anakwaniritsa mau ake adanenawo, kutitsutsa ife ndi oweruza athu otiweruza, ndi kutitengera choipa chachikulu; pakuti pansi pa thambo lonse sipanachitike monga umo panachitikira Yerusalemu.


Udzazidwa nao manyazi m'malo mwa ulemerero; imwa iwenso, nukhale wosadulidwa; chikho cha dzanja lamanja la Yehova chidzatembenukira iwe, ndi kusanza kwa manyazi kudzakhala pa ulemerero wako.


Ndipo chimzinda chachikulucho chidagawika patatu, ndi mizinda ya amitundu inagwa; ndipo Babiloni waukulu unakumbukika pamaso pa Mulungu, kuti aupatse chikho cha vinyo waukali wa mkwiyo wake.


nadzanena, Tsoka, tsoka, mzinda waukulu wovala bafuta ndi chibakuwa, ndi mlangali, wodzikometsera ndi golide ndi mwala wa mtengo wake, ndi ngale!


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa