Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 132:16 - Buku Lopatulika

16 Ndipo ansembe ake ndidzawaveka ndi chipulumutso: Ndi okondedwa ake adzafuulitsa mokondwera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Ndipo ansembe ake ndidzawaveka ndi chipulumutso: Ndi okondedwa ake adzafuulitsa mokondwera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Ansembe ake ndidzaŵaveka chipulumutso, anthu ake oyera mtima adzafuula ndi chimwemwe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 132:16
9 Mawu Ofanana  

Ndipo tsopano nyamukani, Yehova Mulungu, kudza kopumulira kwanu, Inu ndi likasa la mphamvu yanu; ansembe anu, Yehova Mulungu, avale chipulumutso; ndi okondedwa anu akondwere nazo zabwino.


Ansembe anu avale chilungamo; ndi okondedwa anu afuule mokondwera.


Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa; ndisungeni kwa munthu wachiwawa; kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.


Ndidzakondwa kwambiri mwa Yehova, moyo wanga udzakondwerera mwa Mulungu wanga; pakuti Iye wandiveka ine ndi zovala za chipulumutso, nandifunda chofunda cha chilungamo, monga mkwati avala nduwira, ndi monga mkwatibwi adzikometsa yekha ndi miyala yamtengo.


Efuremu andizinga ndi bodza, ndi nyumba ya Israele ndi chinyengo, ndi Yuda apikisana ndi Mulungu, ndiye Woyera wokhulupirika.


Kondwera kwambiri, mwana wamkazi wa Ziyoni; fuula mwana wamkazi wa Yerusalemu; taona, Mfumu yako ikudza kwa iwe; ndiye wolungama, ndi mwini chipulumutso; wofatsa ndi wokwera pabulu, ndi mwana wamphongo wa bulu.


Kufikira tsopano simunapemphe kanthu m'dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikwaniridwe.


Pakuti nonse amene munabatizidwa kwa Khristu mudavala Khristu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa