Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 123:2 - Buku Lopatulika

2 Taonani, monga maso a anyamata ayang'anira dzanja la ambuye wao, monga maso a adzakazi ayang'anira dzanja la mbuye wao wamkazi: Momwemo maso athu ayang'anira Yehova Mulungu wathu, kufikira atichitira chifundo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Taonani, monga maso a anyamata ayang'anira dzanja la mbuye wao, monga maso a adzakazi ayang'anira dzanja la mbuye wao wamkazi: Momwemo maso athu ayang'anira Yehova Mulungu wathu, kufikira atichitira chifundo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Monga momwe anyamata amayang'anira ku dzanja la bwana wao, monga momwe adzakazi amayang'anira ku dzanja la dona wao, ndi momwenso timayang'anira ife kwa Chauta Mulungu wathu, mpaka atatichitira chifundo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo, monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake, choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu, mpaka atichitire chifundo.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 123:2
14 Mawu Ofanana  

Ndipo iye anati Ndileke ndimuke, chifukwa kulinkucha. Ndipo Yakobo anati, Sindidzakuleka iwe kuti umuke, ukapanda kundidalitsa ine.


Ndadikira chipulumutso chanu, Yehova.


Ndipo tsopano, mbuye wanga mfumu, maso a Aisraele onse ali pa inu, kuti muwauze amene adzakhala pa mpando wachifumu wa mbuye wanga mfumu atamuka iye.


Mulungu wathu, simudzawaweruza? Pakuti mwa ife mulibe mphamvu yakulimbana nao aunyinji ambiri awa akutidzera; ndipo sitidziwa ngati tidzatani, koma maso athu ali kwa Inu.


Maso anga anatha mphamvu ndi kukhumba mau anu, ndikuti, Mudzanditonthoza liti?


Maso anga alinga kwa Yehova kosaleka; pakuti Iye adzaonjola mapazi anga mu ukonde.


Ndipo anawanenera fanizo lakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafooka mtima;


Ndipo amuna a ku Gibiyoni anatumira Yoswa mau kuchigono ku Giligala, ndi kuti, Musalekerere akapolo anu; mutikwerere msanga, ndi kutipulumutsa, ndi kutithandiza; pakuti mafumu onse a Aamori, akukhala kumapiri atisonkhanira.


Ndipo tsopano mukhale otembereredwa, palibe mmodzi wa inu adzamasuka wosakhala kapolo, ndi kutemera nkhuni, ndi kutungira madzi nyumba ya Mulungu wanga.


Ndipo tsiku lija Yoswa anawasandutsa akutema nkhuni, ndi otungira madzi msonkhanowo, ndi guwa la nsembe la Yehova, mpaka lero lino, pamalopo akadzasankha.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa