Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 113:5 - Buku Lopatulika

5 Akunga Yehova Mulungu wathu ndani? Amene akhala pamwamba patali,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Akunga Yehova Mulungu wathu ndani? Amene akhala pamwamba patali,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Ndani angalingane ndi Chauta, Mulungu wathu, amene akukhala kumwamba,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 113:5
14 Mawu Ofanana  

Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba; ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo.


Yehova ali mu Kachisi wake woyera, Yehova, mpando wachifumu wake uli mu Mwamba; apenyerera ndi maso ake, ayesa ana a anthu ndi zikope zake.


Mafupa anga onse adzanena, Yehova, afanana ndi Inu ndani, wakulanditsa wozunzika kwa iye amene amposa mphamvu, ndi wozunzika ndi waumphawi kwa iye amfunkhira?


Pakuti kuli yani kuthambo timlinganize ndi Yehova? Afanana ndi Yehova ndani mwa ana a amphamvu?


Ndiye Mulungu, ayenera kumuopa kwambiri mu upo wa oyera mtima, ndiye wochititsa mantha koposa onse akumzinga.


Yehova, Mulungu wa makamu, wamphamvu ndani wonga Inu, Yehova? Ndipo chikhulupiriko chanu chikuzingani.


Inu ndinu wakuchita ufumu pa kudzikuza kwa nyanja; pakuuka mafunde ake muwachititsa bata.


Afanana ndi Inu ndani mwa milungu, Yehova? Afanana ndi Inu ndani, wolemekezedwa, woyera, woopsa pomyamika, wakuchita zozizwa?


Ndipo mpando wachifumu udzakhazikika m'chifundo, ndimo wina adzakhala pamenepo m'zoona, m'chihema cha Davide, nadzaweruza, nadzafunitsa chiweruziro, nadzafulumira kuchita chilungamo.


Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi chithunzithunzi chotani?


Mudzandifanizira Ine ndi yani tsono, kuti ndilingane naye, ati Woyerayo.


Pakuti atero Iye amene ali wamtali wotukulidwa, amene akhala mwachikhalire, amene dzina lake ndiye Woyera, Ndikhala m'malo aatali ndi oyera, pamodzi ndi yense amene ali wa mzimu wosweka ndi wodzichepetsa, kutsitsimutsa mzimu wa odzichepetsa, ndi kutsitsimutsa mtima wa osweka.


Chifukwa palibe akunga Inu, Yehova; muli wamkulu, ndipo dzina lanu lili lalikulu ndi lamphamvu.


Palibe wina ngati Mulungu, Yesuruni iwe, wakuyenda wokwera pathambo, kukuthandiza, ndi pa mitambo mu ukulu wake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa