Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 1:3 - Buku Lopatulika

3 Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Tsono Mulungu adati, “Kuyere,” ndipo kudayeradi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 1:3
22 Mawu Ofanana  

Imeneyo ndiyo mibadwo yao ya zakumwamba ndi dziko lapansi, pamene zinalengedwa, tsiku lomwe Yehova Mulungu anapanga dziko lapansi ndi zakumwamba.


Taonani, Iye ayala kuunika kwake pamenepo. Navundikira kunsi kwake kwa nyanja.


Ili kuti njira yomukira pokhala kuunika? Ndi mdima, pokhala pake pali kuti,


muvala ulemu ndi chifumu. Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi chovala; ndi kuyala thambo ngati nsalu yotchinga.


Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira; mangani nsembe ndi zingwe, kunyanga za guwa la nsembe.


Alemekeze dzina la Yehova; popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.


Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova; ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwake khamu lao lonse.


Pakuti ananena, ndipo chinachitidwa; analamulira, ndipo chinakhazikika.


Kuunika kufesekera wolungama, ndi chikondwerero oongoka mtima.


Ine ndilenga kuyera ndi mdima, Ine ndilenga mtendere ndi choipa, Ine ndine Yehova wochita zinthu zonse zimenezi.


Dzuwa silidzakhalanso kuunika kwako usana, ngakhale mwezi sudzakuunikiranso kuti kuyere; koma Yehova adzakhala kwa iwe kuunika kosatha, ndi Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.


Ndipo Yesu anatambalitsa dzanja lake, namkhudza iye, nati, Ndifuna; takonzedwa. Ndipo pomwepo khate lake linachoka.


Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikire.


Uku ndiko kuunika kwenikweni, kumene kuunikira anthu onse akulowa m'dziko lapansi.


Ndipo m'mene adanena izi, anafuula ndi mau aakulu, Lazaro, tuluka.


Koma chiweruziro ndi ichi, kuti kuunika kunadza kudziko lapansi, ndipo anthu anakonda mdima koposa kuunika; pakuti ntchito zao zinali zoipa.


Pakuti Mulungu amene anati, Kuunika kudzawala kutuluka mumdima, ndiye amene anawala m'mitima yathu kutipatsa chiwalitsiro cha chidziwitso cha ulemerero wa Mulungu pankhope pa Yesu Khristu.


Mwa ichi anena, Khala maso wogona iwe, nuuke kwa akufa, ndipo Khristu adzawala pa iwe.


pakuti kale munali mdima, koma tsopano muli kuunika mwa Ambuye; yendani monga ana a kuunika,


amene Iye yekha ali nao moyo wosatha, wakukhala m'kuunika kosakhozeka kufikako; amene munthu sanamuone, kapena sangathe kumuona; kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu yosatha. Amen.


Ndipo uwu ndi uthenga tidaumva kwa Iye, ndipo tiulalikira kwa inu, kuti Mulungu ndiye kuunika, ndipo mwa Iye monse mulibe mdima.


Ndikulemberaninso lamulo latsopano, ndicho chimene chili choona mwa Iye ndi mwa inu; kuti mdima ulinkupita, ndi kuunika koona kwayamba kuwala.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa