Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Genesis 1:3 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

3 Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Tsono Mulungu adati, “Kuyere,” ndipo kudayeradi.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 1:3
22 Mawu Ofanana  

Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,


Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.


“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?


Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti


Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.


Zonse zitamande dzina la Yehova pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.


Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.


Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.


Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.


Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.


Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.


Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” Nthawi yomweyo anachiritsidwa khate lake.


Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.


Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.


Yesu atanena izi, Iye anayitana ndi mawu ofuwula kuti, “Lazaro, tuluka!”


Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa.


Pakuti Mulungu amene anati, “Kuwala kuwunike kuchokera mu mdima,” Iyeyo ndiye anawunikira mʼmitima mwathu kutipatsa kuwala kuti tidziwe ulemerero wa Mulungu umene ukuoneka pa nkhope ya Yesu Khristu.


Nʼchifukwa chake Malemba akuti, “Dzuka, wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.”


Pajatu inu nthawi ina munali mdima, koma tsopano ndinu kuwunika mwa Ambuye. Mukhale ngati ana akuwunika


Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni.


Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.


Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa